KADYEDWE KOYENERA PA UMOYO WA MUNTHU
Nzosakaikitsa kuti mphindi zingapo zapitazi mwangomaliza kumene kudya chakudya, ndipo mukatha kuwerenga nkhani-yi sizikhala zachilendo kuti Njala ikuimbirani likhweru kuti mudye chakudya chinachake.Koma nkhani yagona pa chakudya choyenera mthupi la munthu. Naomi Mvula, yemwe ndi katswiiri wotsatira kadyedwe ka bwino,watambasula za chakudya chabwino. “Pali zakudya ma gulu asanu ndi limodzi .Zakudya zokhutitsa ; Chinangwa, Mbatata, […]

MALONDA A NYAMA YABWINO
Ngati muli pa Msika, tasuzumirani kumalo ogulitsira nyama kuphatikizapo nyama ya nkhuku. Mugwirizana nane kuti ndiwo ya nyama, ndiyokhayo yomwe imapangitsa phwando kapena mwambo wa Maliro kukhala osimbika. Nthawi zinanso angakhale ku Chilendo kumene akakuphikira nyama, umakhala ndi chimwemwe chodzala mtsaya. A James Simika ,omwe ndi mmodzi mwa anthu ochita Malonda ogulitsa nyama akusimba za […]

MPHAMVU YA NYIMBO ZÀ KU MALAWI
Nyimbo ndi chinthu chimodzi chimene chimapezeka mnyengo zonse za munthu. Mkulu wa bungwe loyanga’anira oyimba mdziko muno la Musicians Union of Malawi ,Vita Chirwa, akufotokoza za momwe mayimbidwe akuyendera. “Maimbidwe kuno kwathu ku Malawi, akupita patsogolo. Taona oyimba kuno kwathu akuitanidwa kupita kukayimba ku Mayiko akunja komanso kuwina photho za padziko lonse”. Vita wayamikira atsogoleri […]

UBWINO WA KUKONZEKERA POCHITA ZINTHU.
Pamene mumatsegula tsambali kuti muwerenge nkhaniyi ,ndiri nacho chikhulupiriro kuti munakonzekera.Munthu umakhala kakasi kapena kusowa mtengo ogwira ngati sunakonzekere pakuchita chinachake.Mbusa Vincent Nguluwe, watambasula kukonzekera kuti ndi kukonzekera zinthu zomwe munthu ukufuna kuti uchite kuti ukafikire china chake. “Kukonzikera kudayamba ndi Mulungu. Genesis 1 ndime ya 1″. Watero , Nguluwe. Mbusayu, wati kukonzekera kumathandizira munthu […]
