PHINDU LA MAPHUNZIRO A CHUMA KU MALAWI
Chuma ndi chinthu chimene chimafunikira kwambiri pa moyo wa munthu aliyense posatengera komwe munthu amachokera. Maphunziro a nkhani za chuma kuno kwathu ndi mnyanga wa njobvu. Katswiri pa nkhani ya zachuma,Innocent Banda watsindika kuti muli phindu mma phunziro a nkhani za chuma”Maphunziro a zachuma ali ndi phindu pa munthu payekha chifukwa Ndalama-zo amazipeza ndi munthu”. […]
KODI CHUMA CHA ZIPANI ZA NDALE CHIMA CHOKA KUTI?
Mawu akuti bongololo sadzolera mafuta pa gulu akugwirizana kwambiri ndi zomwe zipani za ndale zimachita pa nkhani youlula komwe kumachokera chuma chake. Victor Chipofya, yemwe ndi katswiri pa nkhani za ndale wati aMalawi samamvetsetsa momwe ndalama zoyendetsera zipani zimachokera.”Nthawi zambiri Chipani chokuti chiri kotsutsa chikangolowa m’boma chimayamba kugula magalimoto ankhaninkhani.Izi zimadabwitsa kuti ndalama azitenga kuti?.Nchifukwa […]
NYENGO YA MDZIKO LA MALAWI YASANDULIKA
Zovala zomwe anthu timavala zimagwirizana ndi nyengo, ntchito zathu zimene zimachitika malingana ndi Nyengo. Tikawunikira nyengo ya mvula kuno kwathu ku Malawi ,nayo idasintha. Chifundo Dalireni , yemwe ndi mmodzi mwa akatakwe a zachirengedwe watsimikiza kuti nyengo idasintha.”Nyengo idasintha pafupifupi pa dziko lonse lapansi”. Katswiriyu wafotokoza kuti kudula mitengo, kutulutsa utsi kwambiri ku ma fakitale […]
ZOYENERA KUCHITA PA MALO OGWIRA NTCHITO
Malo ogwirira ntchito ali ngati nyambo mmanja mwa mnsodzi ndipo kugwira ntchito kumayika chimwemwe mtsaya pomwe malipiro akuperekedwa.Komatu kuzindikira ntchito yako nkofunika pa Kampani kapena bungwe limene munthu akuligwirira ntchito. Mkulu ochokera ku Bungwe lolimbikitsa luso losiyanasiyana pakati pa achinyamata la CISE Malawi, a Davis Damison, wafotokoza kuti ndikofunikira kwambiri ngati bungwe kapena kampani kudziwa […]