Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist

KAUNIUNI WA MOYO AZICHITIKA NDITHU PA MALAWI

Written by on October 13, 2024

Galimoto za mtidzi, nyumba za pamwamba  komanso zovala zodula  ndi zina mwa zinthu zomwe mtima umafuna utazipeza mmoyowu.Ichi chifukwa  chake pali mkuluwiko wotchedwa ‘mtima Suvala Sanza’.

Davis Damison yemwe ndi mkulu wa Community Initiative for Social Empowerment (CISE)Malawi , wafotokoza kuti kauniuni wa Moyo (life style audit)ndi makhalidwe  a munthu potengera zinthu zimene wapeza kapena kutaya.

Damison wati mbiri ya Ndale ndi utsogoleri  mdziko muno  imati yemwe  adali Mtsogoleri woyamba wa dziko  lino Malemu Dr. Hastings Kamuzu Banda ,adali yekhayo amene ankachita kauniuni munthu akafuna kupanga chitukuko.”Dr Hastings Kamuzu Banda, adali patsogolo kupanga kauniuni  kwa munthu aliyense (wogwira ntchito m’boma olo  Malonda)akafuna kumanga Nyumba yapamwamba.  Chimene amapanga  amafunsidwa munthu uja kuti Ndalama wazitenga kuti ,ukupanga Malonda anji,umagwira ntchito yanji?”. Iye, wati izi zimathandizira kuti munthu akhale ndi popezera ndalama  pogwirika.

Mkulu waku CISE Malawi-yu, wati ndizodandaulitsa kuti  munthu amasintha momwe amakhalira akapatsidwa udindo m’boma kapena ku Chipani. “Anthu amakhala ndi nkhawa anthu a akapatsidwa ma udindo ndipo anthu sangapeze mayankho kaamba ka mphanvu zimene adindo amakhala nazo, makhalidwe akasintha ndipo ndi ntchito yofunika kafukufuku”.

Damison wati kupanga kauniuni nkofunikira kwa munthu pa iye yekha ngakhale Boma  popeza kumapereka chiyembekezo kwa anthu komanso ku Boma. Anthu amakhala ndi chikhulupiliro kuti palibe amene akusakaza misonkho.

Kumbali yothana ndi katangale ndi Ziphuphu  Davis Damison wanena poyera kuti Boma la Mgwirizano wa Tonse sirinayike patsogolo  chidwi chothana ndi katangale.” A Malawi  siwokhutira mmene Bomali likupangira pa nkhani ya Katangale  chifukwa pali milandu yambirimbiri imene a Malawi amaitsatira .Chiyembekezo chawo chinali chokut enieni akupanga katangale azengedwe milandu,chilango chiperekedwe pofuna kupereka phunziro kwa a Malawi ena”. Damison ,watero.Komabe Iye wachita changu kunena kuti ngati Boma pali zinthu zingapo zofuna kuthana ndi katangale. Iye watchulapo ndondomeko  monga kutsegulidwa kwa ofesi ya bungwe la ACB m’boma  la Mchinji.

Iye, wati atsogoleri ambiri amabwezedwa mbuyo  posafuna kusakhala ndi makhalidwe abwino chifukwa adindo ambiri  ali ndi moyo  odziwonetsera pa zinthu zimene alinazo. Mwachitsanzo, kukhala  ndi gulu lotchedwa ma ‘big men’. Malingana  ndi a Damison, achinyamata ambiri amasirira komanso kuwonetsa chidwi chofuna kupikisana nawo pa udindo wa Ndale ndicholinga chofuna kukapeza zinthu ngati  Galimoto  za pamwamba  ati popeza iwowa amaona akuluakulu omwe ali pa maudindo akukhala ndi katundu  wapamwamba  ngakhale kuti akhala pa maudindo kwa nthawi yochepa.

Damison  wati njira yabwino  yodzichitira kauniuni  mmoyo ndi kumvera lamulo  loulula chuma  chomwe munthu wapeza (assert declaration) uli mdindo m’boma. Iye waonjezera kuti nthambi  za Boma monga  Bungwe lothana ndi Katangale ndi Ziphuphu likuyenera kumadziwitsa anthu za ubwino  woulula chuma chawo komanso kuzindikiritsa Mzika za dziko za ntchito  za ma khonsolo, Bwanankubwa ndi komwe kungathandize kusamala chuma cha Boma.

Damison wathokoza atolankhani òmwe amadziwitsa a Malawi kaamba kolemba ndi kudziwitsa anthu za yemwe akuchita Katangale. “Atolankhani akugwira ntchito yotamandika kwambiri kuti tizidziwa kuti zinthu zimene zikuchitika ndi zotani”. Mkulu wa ku CISE  Malawi-yu , wati ambiri  a ndale akukhudzidwa ndi kupindula ku mchitidwe wa Katangale  ndipo ndi atolankhani amene amatidziwitsa.

Malingana ndi Transparency  Corruption  Index, Dziko  la Malawi liri pa nambala 115 pa maiko 180 omwe Katangale adamanga nthenje ndipo liri pa mlingo wa ma pointi makumi atatu ndi mphambu zinayi (34)  pa mapointi zana limodzi(100)pothana ndi katangale ndi Ziphuphu.


Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist