Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist

BUNGWE LA ACB LIKUWODZERA

Written by on October 13, 2024

Ndizosabisa kunena kuti Moto wa khala la Mtengo wa Tsanya omwe umayaka ku Bungwe lothana ndi Katangale ndi Ziphuphu  tsopano uli ngati Moto wa Mapesi.

Katswiri woyankhulapo pa nkhani za Utsogoleri wabwino komanso momwe zinthu zikuyendera mdziko muno   Victor  Chipofya, wati sakumva nkhani  mma Nyuzipepala  ngati momwe zinaliri mbuyomu .”Sitikumva zinthu mma Nyuzipepala ngati mmene timamvera mmene  kunaliri Martha Chizuma, ngati kuchoka kwa a Martha Chizuma kwapangitsa kuti Bungwe lothana ndi Katangale ndi Ziphuphu  la Anti Corruption Bureau (ACB ),lisamagwire ntchito  yawo kapena likhale chete ndizokhumudwitsa kwambiri chifukwa  Bungwe silimagwira ntchito ndi munthu mmodzi.A Chizuma anali wongotsogolera chabe komano kuli anthu ena okuti amakhala akugwira ntchito yawo tsiku ndi tsiku kuwonetsetsa kuti akuthana ndi Katangale ndi Ziphuphu”.

 

Chipofya, sanafune kubisa Mawu ndipo wati bvuto ndilakuti  Bungwe la ACB,  limatsogoza munthu.”Kwa nthawi  yayitali timafuna kuti munthu mmodzi  adziwonekera kwambiri  kusiyana  ndi  Bungwe.Timatchula munthu mmalo motchula kuti Bungwe la ACB  likufufuza kapena lamanga wakuti,  chifukwa chake munthu akachoka kumakhala kuli chete”. Katswiriyu anaonjezera kunena kuti ntchito yomwe amagwira a ACB  ndi ntchito  yoopsya kotero amalimbana ndi anthu amene kwa iwo katangale ndi Mpunga wawo, ndi Chingwa chawo(chakudya chawo cha tsiku ndi tsiku). Iye walangiza kuti sipafunika kuulula dzina la munthu otsogolera ACB ,pamene akufufuza anthu koma kumanena kuti Bungwe ndicholinga chofuna kupewa adani.

 

Katswiri oyankhulapo pa nkhani za Utsogoleri wabwino-yu , wati ndizodetsa nkhawa kwambiri  kuti  kufikira lero Bungwe lothana ndi Katangale ndi Ziphuphu lidakalibe Mtsogoleri  chichokereni a Martha Chizuma. Izi ati zikusonyeza kuti palibe chidwi kwenikweni  chofuna kuthana ndi Katangale ndi Ziphuphu. Iye, wapempha Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera, kuti pachitike machawi kupeza Mtsogoleri wa Bungweli.

 

Victor Chipofya , wati pali chiopsyezo chokuti anthu atha kuyamba kunyinyirika  kupereka misonkho ngati  mabungwe  ena a Boma akuchita zinthu zawo mobisa ponena kuti mabungwe wa amayendetsedwa ndi Misonkho ya a Malawi.

 

Powaika pa mlingo kunkhani yolimbana ndi katangale , a Chipofya  ati a Chakwera  alibe chidwi.” A Pulezidenti akhumudwitsa  mtundu wa a Malawi ku nkhani ya kumenyana ndi Katangale ndi Ziphuphu. Mmene amayankhulira a Pulezidenti asadalowe pa mpando ndi mmene akuchitika zikusonyezeratu kuti alibe chidwi cholimbana ndi Katangale. A Pulezidenti  amaoneka kuti anali ndi chidwi  chomenyana ndi katangale ndi Ziphuphu ali Mtsogoleri wotsutsa Boma”. Chipofya,watero. Mtsogoleri wa dziko lino  yu adalonjeza kudzachepetsa Mphanvu  zake pa nkhani ya kasankhidwe ka mkulu wa Bungwe  la ACB zomwe lero lino ndi Maloto a Chiwumba.

 

Chipofya , watchulapo nkhani ya Ndalama  zomwe zinaperekedwa ku Bakery kuti zikagulidwire feteleza,Ndalama  zina zogulira zipangizo za Ulimi zotsika mtengo zinaperekedwa ku Kampani yopanga Nsalu, komanso ku Bungwe  logula Mafuta a Galimoto mdziko muno  la NOCMA  kudzera kwa Mlembi wa Mkulu  mu ofesi  ya Mtsogoleri wa dziko lino akupanga ziganizo zosemphana ndi mmene zikuyenera kukhalira. Iye, wati palibe  chimene chachitikapo kufuna kuthana  ndi izi.

 

Katswiriyu  wati ngati  pali Boma  limene lidalowa ndi mafuno a bwino kuchokera ku mtundu wa a Malawi  ndi Boma la Mgwirizano wa Tonse,  koma mwayi wa chikhulupiliro cha  Boma-li  watayika ndipo Boma la Mgwirizano wa Tonse  lataya lokha mwayiwu.

 

Victor Chipofya wati Katangale  ali ngati Nthata ndipo Njira yabwino yolimbana ndi katangale ndi Ziphuphu ndikuphunzitsa ana za kuyipa kwa mchitidwewu adakali ku Sukulu  za Pulayimale. Chipofya  waperekanso ganizo lokuti munthu amene  wapezeka  akuchita Katangale  akuyenera kumangidwa,kuzengedwa mlandu ndiponso adzilembedwa mu Nyuzipepala.

 

Mayi Martha Chizuma ,adasankhidwa pa 29 April 2021 kukhala mkulu wa Bungwe lothana ndi katangale ndi Ziphuphu kufikira pa 31 May 2024. Mkatikati mogwira ntchito yawo, a Chizuma  adamangidwa ndi a Police m’mwezi wa September mchaka cha 2023.


Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist