Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist

MALONDA A NYAMA YABWINO

Written by on February 25, 2025

Ngati muli pa Msika, tasuzumirani kumalo ogulitsira nyama kuphatikizapo nyama ya nkhuku. Mugwirizana nane kuti ndiwo ya nyama, ndiyokhayo yomwe imapangitsa phwando kapena mwambo wa Maliro kukhala osimbika. Nthawi zinanso angakhale ku Chilendo kumene akakuphikira nyama, umakhala ndi chimwemwe chodzala mtsaya. A James  Simika ,omwe ndi mmodzi mwa anthu ochita Malonda ogulitsa nyama akusimba za malondawa.

” Timagulitsa mitundu yonse ya nyama ngati ; Nkhuku, Nyama yoperapera kuphatikizaponso Mang’ina.Chibwerereni panopa pa Gulliver (Area 49) mu mdzinda wa Lilongwe,anthu adatidziwa kuti  pa Gulliver  pamene pamakhala Nyama yabwino  ndi pa Tower pano”.  Simika, wafotokoza.

Mkuluyu ,wachenjeza anthu ochita Malonda a butchery kuti adzikhala osamalitsa komanso kusakhala ndi nkhawa iriyonse pamene ochita Malonda-wa akugwiritsa ntchito  mpeni wa makono omwe umagwiritsa ntchito  mphamvu ya magetsi podulira nyama mmiringo yosiyanasiyana.” Ndimakina (mpeni) owopsya. Ena adadukako dzala ndiye pamafunika kusamalitsa ukamagwiritsa ntchito  Mpheni-wu, osatayirira”.

Kumbali ya kayendedwe ka malonda a nyama, James wadandaula kuti kugwa kwa mphamvu ya ndalama ya kwacha mwa kapitikapiti  kwabwezeretsa malonda awo mbuyo. Mkulu ochita malonda-yu waulula kuti  munthu thanks kukhala ndi Filiji zoonekera mkati, mpeni wa makono komanso ng’ombe imodzi  akafuna kuyamba  geni ya nyama.

Pa za mbiri yawo yogulitsa nyama yofewa, James waulula kuti nyama yawo amakagula ku Cold Storage, komanso amayisamalira bwino pamene magetsi athima poti ali ndi generator  zothandizira kuziziritsa Nyama kupyolera mmagetsi ake. Simika, wagwirizana kwa thunthu ndi bungwe loona ndi kuyeza milingo ya zinthu mdziko muno la Malawi Bureau of Standards, kuti ukhondo umafunikira pa malonda  omwe uli ndi kuthekera kokopa anthu ogula.

“Chipongwe kwa kasitomala, komanso bwana wako sizabwino kaamba koti  zimakuika munthu mmavuto ochotsedwa ntchito”. Iye, wachenjeza.  Simika, wati kasitomala amafunika kuchengetedwa ngati mwana komanso osamunyoza akabwera ndi ndalama  yochepa.

James Simika, wamema anthu kuti adzigula nyama pa butchale yawo ya Fresh Food.  Iye, wati amatha kumuotchera nyama  kasitomala mwa ulere akagula nyama pa malowa. Mkuluyu waonjeezera kumema ochita malonda kuti alimbe mtima kuchita geni ngakhale katundu wakwera kwambiri pa msika.


Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist