Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist

MPHAMVU YA NYIMBO ZÀ KU MALAWI

Written by on February 8, 2025

Nyimbo ndi chinthu chimodzi chimene chimapezeka mnyengo zonse  za munthu. Mkulu wa bungwe loyanga’anira oyimba mdziko muno la Musicians  Union of Malawi ,Vita  Chirwa, akufotokoza za momwe mayimbidwe akuyendera.

“Maimbidwe kuno  kwathu  ku Malawi, akupita patsogolo. Taona oyimba  kuno kwathu akuitanidwa kupita kukayimba ku Mayiko akunja komanso kuwina photho za padziko lonse”. Vita wayamikira atsogoleri  a kale a bungweli poika  maziko abwino.

Iye wati ngakhale kuti momwe amabwera pa udindowu mchaka cha 2022, kubwera kwawo  kudabutsa mpungwepungwe popeza anthu ena sanakhutire ndi momwe Masankho adayendera zomwe zidapangitsa kuti Chaka cha 2023 chonse chithe opanda  ntchito  yolozeka.

Bata litadza ku Bungweli(2024), Vita  adakwaniritsa kupanga ubale  ndi Sukulu ya ukachenjede wa Sayansi, ya MUST, kuti adzisinthana zochita kumbali ya Maimbidwe. Kuphatikiza apo , Bungweli  lidalunga ndikuthandiza anthu omwe adakumana ndi Ngozi ya Namondwe  Freddy ,pambali pa ma ubale ena.

Mkuluyu, wati Bungweli  lawo lidalandira  thandizo la ndalama  kuchokera ku Copyright Fund ndi cholinga cholimbikitsa malingaliro a ngwiro pozindikira kupululuka kwa miyoyo ya anthu ongodzipha okha kaamba ka nkhawa.

Iye, wati izi zidachitika kutinso oyimba asamaimbe nyimbo zodandaulitsa.

Pankhani  ya kagwiridwe ntchito  ndi oyimba  nyimbo za chikunja ndi za uzimu, Chirwa watsutsa mphekesera zokuti  kumakhala kovuta kugwirira ntchito  limodzi ndi ma guluwa.” Ku Musicians  Union of Malawi, kulibe tsankho”. Watero, Vita.

Pa tanthauzo la oyimba kukhala kazembe ku bungwe kapena kampani, Vita Chirwa, wati izi zimatanthauza kuti woyimbayo wachita bwino pa Maimbidwe ake kuphatikizapo kuzitsatsa komanso ukadaulo.

Mkulu wa Bungwe la MUM-yu ,wati iye oyimbawa amamvetsetsa pa zomwe akuyenera kukwanilitsa akakhala Kazembe.

Kumbali  ya kusakhutitsidwa kwa Kampani pa zochita za kazembe wake, Chirwa ,  wati pamakhara Mgwirizano ndipo bwalo la Milandu ndilomwe limathetsa kusamvanaku.

Luso la Makono kumbali  yonyamulira uthenga wa Nyimbo, Vita  Chirwa wati malo ngati YouTube pongotchulapo ochepa chabe ndi abwino popeza  amathandizilanso kugulitsa oyimba.

Mkuluyu, wayamikiranso mabwalo oyimba kuti akumakhala abwino komanso anthu akumakhutitsidwa.

Pothirirapo ndemanga  pa kuimba pa Msika wa dziko lonse, Chirwa wati izi zikutanthauza kuti ngati  dziko tikusuntha  ndipo walimbikitsa oyimba kuti adzibwera ndi photho za pamwamba za kunja (Grammy awards ).

Mtsogoleri wa Bungwe la anthu oyimbayu, wapempha anthu oyang’anira  oyimba (managers) kuti asiye  oyimba adzipanga za Nyimbo ndipo manager adzichita mbali yake ngati kusaka malo okaimbira.

Vita Chirwa, wathokoza ndi kuyamikira a Malawi kaamba ka chidwi  ndi chithandizo chimene amapereka kwa oyimba kuno ku Malawi.

Bungwe la Musicians Union of Malawi  (MUM), lidakhazikitsidwa mu 1994 ndipo lidalembetsedwa mwezi wa May ,mu 2002 ndicholinga choteteza ufulu ndi umoyo wa oyimba.


Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist