Blog
Nyimbo ndi chinthu chimodzi chimene chimapezeka mnyengo zonse za munthu. Mkulu wa bungwe loyanga’anira oyimba mdziko muno la Musicians Union of Malawi ,Vita Chirwa, akufotokoza za momwe mayimbidwe akuyendera. “Maimbidwe kuno kwathu ku Malawi, akupita patsogolo. Taona oyimba kuno kwathu akuitanidwa kupita kukayimba ku Mayiko akunja komanso kuwina photho za padziko lonse”. Vita wayamikira atsogoleri […]
Pamene mumatsegula tsambali kuti muwerenge nkhaniyi ,ndiri nacho chikhulupiriro kuti munakonzekera.Munthu umakhala kakasi kapena kusowa mtengo ogwira ngati sunakonzekere pakuchita chinachake.Mbusa Vincent Nguluwe, watambasula kukonzekera kuti ndi kukonzekera zinthu zomwe munthu ukufuna kuti uchite kuti ukafikire china chake. “Kukonzikera kudayamba ndi Mulungu. Genesis 1 ndime ya 1″. Watero , Nguluwe. Mbusayu, wati kukonzekera kumathandizira munthu […]
Zolemba zambiri zimafotokoza kuti ulimi ndi kudzala mbewu komanso kuweta zifuyo pa Malo ogwiritsidwa ntchito ndi anthu. Mutha kututumuka mutamva kuti ulimi ndi kudzala mbewu, kuweta Nyama ndi kubzala mitengo, pozisamalira ndi kuikolola. Musatutumuke ndi zomwe mwamvazi popeza izi ndi zochitika ndithu. Mkulu wa kampani ya Headman Nursery , Elijah Nyirenda ochokera ku Nkhatabay, wafotokoza […]
Chuma ndi chinthu chimene chimafunikira kwambiri pa moyo wa munthu aliyense posatengera komwe munthu amachokera. Maphunziro a nkhani za chuma kuno kwathu ndi mnyanga wa njobvu. Katswiri pa nkhani ya zachuma,Innocent Banda watsindika kuti muli phindu mma phunziro a nkhani za chuma”Maphunziro a zachuma ali ndi phindu pa munthu payekha chifukwa Ndalama-zo amazipeza ndi munthu”. […]
Mawu akuti bongololo sadzolera mafuta pa gulu akugwirizana kwambiri ndi zomwe zipani za ndale zimachita pa nkhani youlula komwe kumachokera chuma chake. Victor Chipofya, yemwe ndi katswiri pa nkhani za ndale wati aMalawi samamvetsetsa momwe ndalama zoyendetsera zipani zimachokera.”Nthawi zambiri Chipani chokuti chiri kotsutsa chikangolowa m’boma chimayamba kugula magalimoto ankhaninkhani.Izi zimadabwitsa kuti ndalama azitenga kuti?.Nchifukwa […]
Zovala zomwe anthu timavala zimagwirizana ndi nyengo, ntchito zathu zimene zimachitika malingana ndi Nyengo. Tikawunikira nyengo ya mvula kuno kwathu ku Malawi ,nayo idasintha. Chifundo Dalireni , yemwe ndi mmodzi mwa akatakwe a zachirengedwe watsimikiza kuti nyengo idasintha.”Nyengo idasintha pafupifupi pa dziko lonse lapansi”. Katswiriyu wafotokoza kuti kudula mitengo, kutulutsa utsi kwambiri ku ma fakitale […]
Malo ogwirira ntchito ali ngati nyambo mmanja mwa mnsodzi ndipo kugwira ntchito kumayika chimwemwe mtsaya pomwe malipiro akuperekedwa.Komatu kuzindikira ntchito yako nkofunika pa Kampani kapena bungwe limene munthu akuligwirira ntchito. Mkulu ochokera ku Bungwe lolimbikitsa luso losiyanasiyana pakati pa achinyamata la CISE Malawi, a Davis Damison, wafotokoza kuti ndikofunikira kwambiri ngati bungwe kapena kampani kudziwa […]
Mutha kuvomerezana nane kuti mwasiya kaye zimene mumachita ndipo mukuwerenga nkhani iyiyi. Mukamaliza, muzikonzekeretsa kuchita zinthu zina. Izi ndi chimodzimodzi ndi kuzikonzekeretsa mmoyo omwe mungakhale mutapuma pa ntchito kapena bizinezi. Benard Chiluzi, mphunzitsi wa kayendetsedwe kabwino ka chuma kuchokera ku old mutual, wadandaulira a Malawi kuti adzikhala akuikiza ndalama ngati njira imodzi yozikonzekeretsa kupuma pa […]
Zamoyo zirizonse zimayenera kulandira chakudya cha bwino kuti zidzikula ndi thanzi. Nayo mbewu ndi chimodzi mwa zinthu za Moyo zomwe zimafuna zakudya zabwino.A Tyson Chapuma, yemwe ndi Mlangizi pa nkhani za Ulimi ku Lunyangwa research station m’boma la Mzuzu , wati akugwira ntchito usiku ndi usana kufufuza za chakudya cha mbewu mu nthaka. Pothirirapo mulomo […]
Next Level Academy, a renowned initiative from the United States of America , has praised Malawi for making significant strides in the creative arts industry. The sentiments were shared by MeccaGodZilla, the team leader for Next Level Academy, during a 10-day masterclass and workshop being held in Lilongwe. The workshop is designed to provide intensive […]