Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist

CHIMWEMWE MU ULIMI WA MITENGO

Written by on February 1, 2025

Zolemba zambiri  zimafotokoza kuti ulimi ndi kudzala mbewu komanso kuweta zifuyo pa Malo ogwiritsidwa ntchito ndi anthu. Mutha kututumuka mutamva kuti ulimi  ndi kudzala mbewu, kuweta Nyama ndi kubzala mitengo, pozisamalira ndi kuikolola. Musatutumuke ndi zomwe mwamvazi popeza izi ndi zochitika ndithu. Mkulu wa  kampani ya Headman Nursery , Elijah Nyirenda ochokera ku Nkhatabay, wafotokoza za ‘malesa’ opezeka mu ulimi wa mitengo.

Iwo ngati  Kampani, adaika chidwi popanga pine ndi bluegum  wa Makono kaamba ka kusakazika kwa mitengo  mu nkhalango ya Chikangawa.”Timapanga mitengo ya pine ndi bluegum wa Makono imene imakula msanga”. Watsindika, Nyirenda.

“Tikudziwa tonse ngati  dziko la Malawi  takhala tikutumiza mitengo  mbuyomu kupita ku Mayiko ena (Tanzania,Uganda,Kenya), koma pano  ndi zachisoni kuti mitengo  ikuchokera kunja chonsecho mitengo tiri nayo konkuno”. Elijah, wadandaula.

Nkuluyu, wati ubwino wa ulimi  wa mitengo  muli phindu lamnanu  popeza siimathiridwa Feteleza kapena  manyowa, siimafuna kuthirira, imakula  msanga komanso . Nyirenda  wati mitengoyi, imangofuna kupalira poipewetsa ku moto  komanso kuitengulira. Iye, wafotokoza  kuti ulimiwu umangofuna munda komanso mitengoyo ngati mpamba.

Kampaniyi, yadandaula kaamba koti Boma silikulimbikitsa komanso kuphunzitsa anthu za ulimi wa mitengo  omwe ungathandiza kubweretsa Ndalama za Kunja. Mkulu wa Kamaniyi, wapempha  Boma kuti  liyambe kuphunzitsa anthu za  ulimi  wa mitengo  ya makonoyi , yomwe imakhwima ndi kukololedwa pakatha  zaka za pakati pa zosachepera zisanu komanso zosapiririra khumi.

Elijah, wati mtengo  wa bluegum  umalola  nthaka  ina iriyonse mdziko muno pamene  Mtengo  wa Pine ,sikawirikawiri kulola nthaka  ya miyala. Mkuluyu  watsindika kuti munthu utha upindula kwakukulu ndi ulimiwu . Mwachitsanzo, malo okwana hekitala imodzi,imatulutsa mitengo ya  Pine okwana  3100,  pamene Mitengo ya bluegum  imalowa yokwanira 2700 pa hekitala imodzi.

Kunkhani yopirira poyembekezera kukolola mitengoyi, Nyirenda  wati  munthu sakuyenera  kungopinda manja uku akudikira kukolola koma atha kupitiriza kumagwira ntchito  zina uku mitengoyo  ikukula kudikira nthawi  yokolola.

Elijah, walosera kuti dziko la Malawi,  litha kukhala  limodzi mwa Maiko opeza Ndalama  zochuluka kwambiri  kuposa maiko  a mu Africa, kudzera mu ulimi  wa mitengo-wu(kugulitsa matabwa kunja). Iye, wati  zotsatira za Ngozi za chilengedwe zogwa mwa dzidzidzi zobwera chifukwa cha kusintha kwa Nyengo ,kutha kukhala kochepepetsedwa ndi Ulimiwu.

Pankhani  ya kulowerera kwa Ndale ku Ulimi  osiyanasiyana, Nyirenda  ,wati izi ndi zodandaulitsa popeza atsogoleri a Ndale  amangokhala ndi Masomphenya a zaka zisanu zokha  mmalo moika chitukuko patsogolo. Iye, wapempha  a Ndale  kuti asamalowerere ndicholinga chobwezera mbuyo chitukuko, ndipo waunikira Boma kuti lisakhazikike potsegula Minda ikuluikulu  ndi cholinga chodzala chimanga kapena soya zokha  komanso Minda ina idzalidwe mitengo ya makonoyi.

Elijah Nyirenda, wamema anthu mdziko muno kuti ayambe ulimi wa mitengo.

Dziko la Malawi, liri ndi ma Hekitala 90,000 a Nkhalango ku Chikangawa, ndipo mitengo yambiri  mu Nkhalangoyi yatha kaamba kodyetsera ziweto, kumanga nyumba zogonamo za malonda, kulima pambali pa zinthu zina zomwe zachepetsa mitengo  Mnkhalangoyi.


Kasupe Radio Live

Kasupe Radio Live

Current track

Title

Artist